Yobu 25
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mawu a Bilidadi
25 Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu,
Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
3 Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka?
Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
4 Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu?
Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
5 Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni,
ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
6 nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi,
mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.